Levitiko 14:19-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo wansembe apereke nsembe yaucimo, namcitire comtetezera amene akuti ayeretsedwe, cifukwa ca kudetsedwa kwace; ndipo atatero aphe nsembe yopsereza;

20. ndipo wansembe atenthe nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa pa guwa la nsembe; ndipo wansembe amcitire comtetezera, ndipo adzakhala iye woyera.

21. Ndipo akakhala waumphawi cosafikana cuma cace azitenga mwana wa nkhosa mmodzi wamwamuna akhale nsembe yoparamula, aiweyule kumcitira comtetezera, ndi limodzi la magawo khumi la efa la ufa wosalala, wosanganiza ndi mafuta, ukhale nsembe yaufa, ndi muyeso umodzi wa mafuta;

22. ndi njiwa ziwiri, kapena maunda awiri, monga akhoza kufikana; limodzi likhale la nsembe yaucimo, ndi linzace la nsembe yopsereza.

Levitiko 14