Levitiko 13:38-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

38. Ndipo ngati mwamuna kapena mkazi ali ndi zikanga pa khungu la thupi lace, zikanga zoyerayera;

39. wansembe aziona; ndipo taonani ngati zikanga ziri pa khungu la thupi lao zikhala zotuwatuwa; ndilo thuza labuka pakhungu; ndiye woyera.

40. Ndipo ngati tsitsi la munthu lathothoka, ndiye wadazi; koma woyera.

41. Ndipo ngati tsitsi lathothoka pamphumi pace ndiye wa masweswe, koma woyera.

Levitiko 13