Levitiko 13:26-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma akaonapo wansembe, ndipo taonani, mulibe tsitsi loyera m'cikangamo, ndipo sicikumba kubzola khungu, koma cazimba; pamenepo wansembe ambindikiritse masiku asanu ndi awiri;

27. ndipo wansembe amuone tsiku lacisanu ndi ciwiri; ngati cakula pakhungu, wansembe amuche wodetsedwa; ndiyo nthenda yakhate,

28. Ndipo ngati cikanga ciima pomwepo, cosakula pakhungu koma cazimba; ndico cotupa ca kupsya; ndipo wansembe amuche woyera; pakuti ndico cipsera ca kupsya.

Levitiko 13