Levitiko 13:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. pamenepo wansembe aone, ndipo taonani, ngati khate lakuta thupi lace, amuche woyera wanthendayo; patuwa ponsepo; ndiye woyera.

14. Koma tsiku liri lonse ukaoneka pa iye mnofu wofiira, adzakhala wodetsedwa,

15. Ndipo wansembe aone mnofu wofiirawo, namuche wodetsedwa; mnofu wofiira ndiwo wodetsa; ndilo khate.

16. Kapena mnofu wofiira ukasandukanso, nusandulika wotuwa, afike kwa wansembe,

17. ndi wansembe amuone, ndipo taonani, ngati nthenda yasandulika yotuwa, wansembe amuche woyera wanthendayo; ndiye woyera.

Levitiko 13