Hoseya 9:5-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Mudzacitanji tsiku la masonkhano oikika, ndi tsiku la madyerero a Yehova?

6. Pakuti taonani, anacokera cionongeko, koma Aigupto adzawasonkhanitsa, Mofi adzawaika m'manda; khwisa adzalanda zofunika zao zasiliva; minga idzakhala m'mahema mwao.

7. Masiku a kulanga afika, masiku a kubwezera afika; Israyeli adzadziwa; mneneri ali wopusa, munthu wamzimu ali wamisala, cifukwa ca kucuruka mphulupulu yako, ndi popeza udani ndi waukuru.

8. Efraimu ndiye wozonda kwa Mulungu wanga; kunena za mneneri, msampha wa msodzi uli m'njira zace zonse, ndi udani m'nyumba ya Mulungu wace.

Hoseya 9