Hoseya 2:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo ndidzampatsa minda yace yamphesa kuyambira pomwepo, ndi cigwa ca Akori cikhale khomo la ciyembekezo; ndipo adzabvomereza pomwepo monga masiku a ubwana wace, ndi monga tsiku lokwera iye kuturuka m'dziko la Aigupto.

16. Ndipo kudzakhala tsiku lomwelo, ati Yehova, udzandicha Mwamuna wanga, osandichanso Baala wanga.

17. Pakuti ndidzacotsa maina a Abaala m'kamwa mwace; ndipo silidzakumbukikanso dzina lao.

18. Ndipo tsiku lomwelo ndidzawacitira pangano ndi nyama za kuthengo, ndi mbalame za mlengalenga, ndi zokwawa pansi; ndipo ndidzatyola uta, ndi lupanga, ndi nkhondo, zicoke m'dziko, ndi kuwagonetsa pansi mosatekeseka.

Hoseya 2