15. Ndipo ndidzampatsa minda yace yamphesa kuyambira pomwepo, ndi cigwa ca Akori cikhale khomo la ciyembekezo; ndipo adzabvomereza pomwepo monga masiku a ubwana wace, ndi monga tsiku lokwera iye kuturuka m'dziko la Aigupto.
16. Ndipo kudzakhala tsiku lomwelo, ati Yehova, udzandicha Mwamuna wanga, osandichanso Baala wanga.
17. Pakuti ndidzacotsa maina a Abaala m'kamwa mwace; ndipo silidzakumbukikanso dzina lao.
18. Ndipo tsiku lomwelo ndidzawacitira pangano ndi nyama za kuthengo, ndi mbalame za mlengalenga, ndi zokwawa pansi; ndipo ndidzatyola uta, ndi lupanga, ndi nkhondo, zicoke m'dziko, ndi kuwagonetsa pansi mosatekeseka.