Hoseya 13:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Israyeli, cikuononga ndi ici, cakuti utsutsana ndi Ine, cithandizo cako.

10. Iri kuti mfumu yako tsopano, kuti ikupulumutse m'midzi yako yonse? ndi oweruza ako amene unanena za iwo, Ndipatseni mfumu ndi akalonga?

11. Ndinakupatsa mfumu mu mkwiyo wanga; ndinamcotsanso m'ukali wanga.

12. Mphulupulu ya Efraimu yamangika, cimo lace lisungika.

13. Zowawa zonga za mkazi wobala zidzamgwera, ndiye mwana wopanda nzeru; pakuti pali nyengo yakuti asacedwe mobalira ana.

Hoseya 13