Hoseya 11:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamene Israyeli anali mwana, ndinamkonda, ndinaitana mwana wanga ali m'Aigupto.

2. Monga anawaitana, momwemo anawacokera; anaphera nsembe Abaala, nafukizira mafano osema.

3. Koma Ine ndinaphunzitsa Efraimu kuyenda, ndinawafungata m'manja mwanga; koma sanadziwa kuti ndinawaciritsa.

Hoseya 11