Genesis 6:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Ndipo Mulungu anaona dziko lapansi, ndipo taonani, linabvunda; pakuti anthu onse anabvunditsa njira yao pa dziko lapansi.

13. Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, Cimariziro cace ca anthu onse cafika pamaso panga; pakuti dziko lapansi ladzala ndi ciwawa cifukwa ca iwo; taonani, ndidzaononga iwo pamodzi ndi dziko lapansi.

14. Udzipangire wekha cingalawa ca mtengo wanjale; upangemo zipinda m'cingalawamo, ndipo upake ndi utoto m'kati ndi kunja.

Genesis 6