10. Ndodo yacifumu siidzacoka mwa Yuda,Kapena wolamulira pakati pa mapazi ace,Kufikira atadza Silo;Ndipo anthu adzamvera iye.
11. Adamanga mwana wa kavalo wace pampesa,Ndi mwana wa buru wace pa mpesa wosankhika;Natsuka malaya ace m'vinyo,Ndi copfunda cace m'mwazi wa mphesa.
12. Maso ace adzafiira ndi vinyo,Ndipo mana ace adzayera ndi mkaka.
13. Zebuloni adzakhala m'doko la kunyanja;Ndipo iye adzakhala doko la ngalawa;Ndipo malire ace adakhala pa Zidoni.