5. Ndipo Farao anati kwa Yosefe, Atate wako ndi abale ako afika kwa iwe;
6. dziko la Aigupto liri pamaso pako: uwakhazike atate wako ndi abale ako pa dera lokometsetsa la dziko; akhale m'dziko la Goseni; ndipo ngati udziwa anthu anzeru a mwa iwo, uwaike iwo ayang'anire ng'ombe zanga.
7. Ndipo Yosefe analowa naye Yakobo atate wace, namuika iye pamaso pa Farao; ndipo Yakobo anamdalitsa Farao.
8. Ndipo Farao anati kwa Yakobo, Masiku a zaka za moyo wanu ndi angati?
9. Ndipo Yakobo anati kwa Farao, Masiku a zaka za ulendo wanga ndi zaka zana limodzi kudza makumi atatu; masiku a zaka za moyo wanga ali owerengeka ndi oipa, sanafikire masiku a zaka za moyo wa makolo angam'masikua ulendowao.
10. Ndipo Yakobo anamdalitsa Farao, naturuka pamaso pa Farao.