Genesis 47:29-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. Ndipo nthawi inayandikira kuti Israyeli adzafa, ndipo anaitana Yosefe mwana wace wamwamuna, nati kwa iye, Ngati ndapeza ufulu pamaso pako, ikatu dzanja lako pansi pa ncafu yanga, nundicitire ine zabwino ndi zoona: usandiikatu ine m'Aigupto;

30. koma pamene ndidzagona ndi makolo anga, udzanditenge ine kuturuka m'dziko la Aigupto, ukandiike ine m'manda mwao. Ndipo iye anati, Ndidzacita monga mwanena.

31. Ndipo anati, Undilumbirire ine; namlumbirira iye. Ndipo Israyeli anawerama kumutu kwa kama.

Genesis 47