8. Ndipo Yosefe anazindikira abale ace, koma iwo sanamzindikira iye.
9. Ndipo Yosefe anakumbukira maloto amene analoto za iwo, ndipo anati kwa iwo, Ozonda inu; mwadzera kudzaona usiwa wa dziko.
10. Ndipo iwo anati kwa iye, Iai, mbuyanga, koma akapolo anu adzera kudzagula cakudya.
11. Tonse tiri ana amuna a munthu mmodzi; tiri oona, akapolo anu, sitiri ozonda.
12. Ndipo iye anati kwa iwo, Iai, koma mwadzera kuti muone usiwa wa dziko.
13. Nati iwo, Akapolo anu ndife abale khumi, ana amuna a munthu mmodzi m'dziko la Kanani; ndipo, taonani, wamng'ono ali ndi atate wathu lero; ndipo palibe mmodzi.
14. Ndipo Yosefe anati kwa iwo, dico cimene ndinakunenani inu, kuti, Ndinu ozonda.