Genesis 38:19-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

19. Ndipo mkazi anauka nacoka, nabvula copfunda cace, nabvala zobvala zamasiye zace.

20. Ndipo Yuda anatumiza kamwana ka mbuzi ndi dzanja la bwenzi lace Madulami, kuti alandire cikole pa dzanja la mkazi; koma sanampeza iye.

21. Ndipo anafunsa amuna a pamenepo kuti, Ali kuti wadama uja anali pambali pa njira pa Enaimu? ndipo iwo anati, Panalibe wadama pano.

22. Ndipo iye anabwera kwa Yuda nati, Sitinampeza mkazi; ndiponso amuna a pamenepo anati, Panalibe wadama pano.

23. Ndipo Yuda anati, Azilandire kuti tingacitidwe manyazi: taona, ndinatumiza mwana uyu wa mbuzi, ndipo sunampeza iye.

24. Ndipo panali itapita miyezi itatu, anamuuza Yuda kuti, Tamara mpongozi wako wacita cigololo, ndiponso taonani, ali ndi pakati ndi cigololoco. Ndipo Yuda anati, Mturutse iye kuti amponye pamoto.

25. Pamene anamturutsa Iye, mkazi anatumiza kwa mpongozi wace kuti, Ndi mwamuna mwini izi ndatenga pakati; ndipo mkazi anati, Tayang'anatu, za yani zimenezi, mphete, ndi cingwe, ndi ndodo?

Genesis 38