Genesis 37:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo abale ace anaona kuti atate wace anamkonda iye koposa abale ace onse: ndipo anamuda iye, ndipo sanathe kulankhula ndi iye mwamtendere.

5. Yosefe ndipo analota loto, nawafotokozera abale ace; ndipo anamuda iye koposa.

6. Ndipo iye anati kwa iwo, Tamvanitu loto limene ndalota:

7. pakuti taonani, ndinalinkumanga mitolo m'munda, ndipo taonani, mtolo wanga unauka nuima ciriri! ndipo taonani, mitolo yanu inadza niuzinga kwete, niuweramira mtolo wanga.

Genesis 37