Genesis 30:41-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Ndipo panali pamene zoweta zolimba zidatenga mabere, Yakobo anaika nthyole pamaso pa zoweta m'miceramo kuti zitenge mabere pa nthyolezo.

42. Koma pamene ziweto zinali zofoka, sanaziika zimenezo: ndipo zofoka zinali za Labani, ndi zolimba zinali za Yakobo.

43. Munthuyo ndipo anakula kwambiri, nali nazo zoweta zambiri, ndi akapolo amuna ndi akazi, ndi ngamila, ndi aburu.

Genesis 30