41. Ndipo panali pamene zoweta zolimba zidatenga mabere, Yakobo anaika nthyole pamaso pa zoweta m'miceramo kuti zitenge mabere pa nthyolezo.
42. Koma pamene ziweto zinali zofoka, sanaziika zimenezo: ndipo zofoka zinali za Labani, ndi zolimba zinali za Yakobo.
43. Munthuyo ndipo anakula kwambiri, nali nazo zoweta zambiri, ndi akapolo amuna ndi akazi, ndi ngamila, ndi aburu.