Genesis 21:5-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ndipo Abrahamu anali wa zaka zana limodzi pamene anambadwira iye Isake mwana wace.

6. Ndipo Sara anati, Mulungu anandisekeretsa ine; onse akumva adzasekera pamodzi ndi ine.

7. Ndipo anati, Akadatero ndani kwa Abrahamu kuti Sara adzayamwitsa ana? pakuti ndambalira iye mwana wamwamuna m'ukalamba wace.

8. Ndipo anakula mwanayo naletsedwa kuyamwa: ndipo Abrahamu anakonza madyerero akuru tsiku lomwe analetsedwa Isake kuyamwa.

9. Ndipo Sara anaona mwana wace wamwamuna wa Hagara M-aigupto, amene anambalira Abrahamu, alinkuseka.

10. Cifukwa cace anati kwa Abrahamu, Cotsa mdzakazi uyo, ndi mwana wace wamwamuna; cifukwa mwana wa mdzakazi uyo sadzalowa m'nyumba pamodzi naye mwana wanga Isake.

11. Ndipo mauwo anaipira Abrahamu cifukwa ca mwana wace.

Genesis 21