Filemoni 1:11-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. amene kale sanakupindulira, koma tsopano watipindulira bwino iwe ndi ine;

12. amene ndi yemweyo ndakubwezera iwe, ndiye mtima weni weni wa ine.

13. Ameneyo ndikadafuna ine kumsunga akhale nane, kuti m'malo mwako akadanditumikira ine m'ndende za Uthenga Wabwino:

14. koma wopanda kudziwa mtima wako sindinafuna kucita kanthu; kuti ubwino wako usakhale monga mokakamiza, komatu mwaufulu.

15. Pakuti kapena anasiyanitsidwa ndi iwe kanthawi cifukwa ca ici, ndi kuti udzakhala naye nthawi zonse;

16. osatinso monga kapolo, koma woposa kapolo, mbale wokondedwa, makamaka ndi ine, koma koposa nanga ndi iwe, m'thupi, ndiponso mwa Ambuye.

Filemoni 1