2. Kutengako malo opatulika akhale nayo mikono mazana asanu m'litali mwace, ndi mazana asanu kupingasa kwace, lamphwamphwa pozungulira pace; ndi pabwalo pace poyera pozungulira pace mikono makumi asanu.
3. Ndipo kuyambira poyesedwapo uyese zikwi makumi awiri mphambu zili sanu m'litali mwace, ndi zikwi khumi kupingasa kwace; m'menemo ndimo mukhale malo opatulika, ndiwo opatulika, ndiwo opatulikitsa.
4. Ndilo gawo lopatulika la dziko, ndilo la ansembe atumiki a malo opatulika, amene ayandikira kutumikira Yehova; apo ndipo amange nyumba zao, likhale malo a pa okha a: kwa malo opatulika.
5. Ndipo zikwi makumi awiri mphambu zisanu m'litali mwace, ndi zikwi khumi kupingasa kwace, ndilo gawo la Alevi, atumiki a kacisi; likhale lao lao la midzi yokhalamo.