Ezekieli 3:2-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Pamenepo ndinatsegula pakamwa panga ndipo anandidyetsa mpukutuwo.

3. Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, dyetsa m'mimba mwako, nudzaze matumbo ako ndi mpukutu uwu ndakupatsawu. M'mwemo ndinaudya, ndi m'kamwa mwanga munazuna ngati uci.

4. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, Muka, nufike kwa nyumba ya Israyeli, nunene nao mau anga.

5. Pakuti sutumizidwa kwa anthu a cinenedwe cosamveka ndi cobvuta, koma kwa nyumba ya Israyeli;

6. si kwa mitundu yambiri ya anthu a cinenedwe cosamveka ndi cobvuta, amene sukhoza kudziwitsa cinenedwe cao. Zedi ndikakutumiza kwa iwowa adzamvera iwe.

7. Koma nyumba ya Israyeli siidzakumvera, pakuti siifuna kundimvera Ine; pakuti nyumba yonse ya Israyeli ndiyo yolimba mutu ndi youma mtima.

8. Taona ndakhwimitsa nkhope yako itsutsane nazo nkhope zao; ndalimbitsanso mutu wako utsutsane nayo mitu yao.

Ezekieli 3