6. cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Popeza waika mtima wako ngati mtima wa Mulungu;
7. cifukwa cace taona, ndidzakufikitsira alendo oopsa a mitundu ya anthu, iwo adzasololera malupanga ao nzeru zako zokongola, nadzaipsa kunyezimira kwako.
8. Adzakutsitsira kumanda, nudzafa mafedwe a ophedwa m'kati mwa nyanja.
9. Kodi udzanena ndithu pamaso pa iye wakupha iwe, Ine ndine Mulungu, pokhala uli munthu, wosati Mulungu, m'dzanja la iye wakupha iwe.
10. Udzafa mafedwe a osadulidwa ndi dzanja la alendo, pakuti ndacinena, ati Ambuye Yehova.
11. Nandidzeranso mau a Yehova, akuti,