Ezekieli 26:1-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali caka cakhumi ndi cimodzi, tsiku loyamba la mwezi, anandidzera mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, popeza Turo ananyodola Yerusalemu, ndi kuti, Onyo, watyoka uwu udali cipata ca mitundu ya anthu; wanditembenukira ine; ndidzakhuta ine, wapasuka uwu;

3. cifukwa cace atero Ambuye Yehova, Taona ndikutsutsa iwe, Turo, ndidzakukweretsera amitundu, monga nyanja iutsa mafunde ace.

4. Ndipo adzagumula malinga a Turo, ndi kugwetsa nsanja zace; inde ndidzausesa pfumbi lace, ndi kuuyesa pathanthwe poyera.

5. Udzakhala poyanika khokapakati pa nyanja, pakuti Ine ndacinena, ati Ambuye Yehova; ndipo udzakhala cofunkha ca amitundu.

6. Ndi ana ace akazi okhala kumunda adzaphedwa ndi lupanga; motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

7. Pakuti atero Ambuye Yehova, Taona ndidzafikitsira Turo Nebukadirezara mfumu ya ku Babulo, mfumu ya mafumu, yocokera kumpoto ndi akavalo, ndi magareta, ndi apakavalo, ndi msonkhano wa anthu ambiri.

Ezekieli 26