Ezekieli 2:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, khala ciriri, ndipo ndidzanena nawe.

2. Ndipo unandilowa mzimu pamene ananena nane, ndi kundiimika ndikhale ciriri; ndipo ndinamumva Iye wakunena nane.

3. Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, ndikutumizira kwa ana a Israyeli, kwa mitundu ya anthu opanduka, amene anapandukana nane; iwo ndi makolo ao anandilakwira mpaka lero lomwe.

4. Ndipo anawa, ndiwo acipongwe ndi ouma mtima, ndikutumiza kwa iwo; ndipo ukanene nao, Atero Yehova Mulungu.

5. Ndipo iwowa, ngakhale akamva kapena akaleka kumva, (pakuti ndiwo nyumba yopanduka,) koma adzadziwa kuti panali mneneri pakati pao.

Ezekieli 2