Ezekieli 2:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, khala ciriri, ndipo ndidzanena nawe.

2. Ndipo unandilowa mzimu pamene ananena nane, ndi kundiimika ndikhale ciriri; ndipo ndinamumva Iye wakunena nane.

3. Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, ndikutumizira kwa ana a Israyeli, kwa mitundu ya anthu opanduka, amene anapandukana nane; iwo ndi makolo ao anandilakwira mpaka lero lomwe.

Ezekieli 2