1. Ndipo anati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, khala ciriri, ndipo ndidzanena nawe.
2. Ndipo unandilowa mzimu pamene ananena nane, ndi kundiimika ndikhale ciriri; ndipo ndinamumva Iye wakunena nane.
3. Nati kwa ine, Wobadwa ndi munthu iwe, ndikutumizira kwa ana a Israyeli, kwa mitundu ya anthu opanduka, amene anapandukana nane; iwo ndi makolo ao anandilakwira mpaka lero lomwe.