53. Ndipo ndidzabweza undende wao, undende wa Sodomu ndi ana ace, ndi undende wa Samariya ndi ana ace, ndi undede wa andende ako pakati pao;
54. kuti usenze manyazi ako, ndi kuti ucite manyazi cifukwa ca zonse unazicita pakuwatonthoza.
55. Ndipo abale ako Sodomu ndi ana ace adzabwerera umo unakhalira kale; ndi iwe ndi ana ako mudzabwerera umo munakhalira kale.
56. Ndipo sunakamba za mbale wako Sodomu pakamwa pako tsiku la kudzikuza kwako;
57. cisanabvundukuke coipa cako monga nthawi ya citonzo ca ana akazi a Aramu, ndi onse akumzungulira iye, ana akazi a Afilisti akupeputsa pozungulira ponse.