Ezekieli 16:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Anandidzeranso mau a Yehova, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, Dziwitsa Yerusalemu zonyansa zace, nuziti,

3. Atero Ambuye Yehova kwa Yerusalemu, Ciyambi cako ndi kubadwa kwako ndiko ku dziko la Akanani; atate wako anali M-amori, ndi mai wako Mhiti.

4. Ndipo za kubadwa kwako, tsiku lobadwa iwe sanadula ncofu yako, sanakuyeretsa ndi kukusambitsa ndi madzi, sanakuthira mcere konse, kapena kukukulunga m'nsaru ai.

Ezekieli 16