Ezekieli 14:9-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo akaceteka mneneriyo, nakanena mau, Ine Yehova ndamceta mneneri uja; ndipo ndidzamtambasulira dzanja langa, ndi kumuononga pakati pa anthu anga Israyeli.

10. Ndipo adzasenza mphulupulu yao, mphulupulu ya mneneri idzanga mphulupulu ya uja wamfunsira;

11. kuti nyumba ya Israyeli isasocerenso kusatsata Ine, kapena kudzidetsanso ndi zolakwa zao zonse; koma kuti akhale anthu anga, ndipo ndikhale Ine Mulungu wao, ati Ambuye Yehova.

Ezekieli 14