1. Pamenepo anafika kwa ine akulu ena a Israyeli nakhala pansi pamaso panga.
2. Ndipo anandidzera mau a Yehova, akuti,
3. Wobadwa ndi munthu iwe, anthu awa anautsa mafano ao mumtima mwao, naimika cokhumudwitsa ca mphulupulu yao pamaso pao; ndifunsidwe nao konse kodi?