1. Ndipo mau a Yehova anandidzera ine, akuti,
2. Wobadwa ndi munthu iwe, Unenere za aneneri a Israyeli onenerawo, nuziti nao onenera za m'mtima mwao mwao, Tamverani mau a Yehova.
3. Atero Ambuye Yehova, Tsoka aneneri opusawo akutsata mzimu wao wao, cinkana sanaona kanthu.
4. Aneneri ako, Israyeli, akhala ngati nkhandwe m'mapululu.