Ezekieli 13:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo mau a Yehova anandidzera ine, akuti,

2. Wobadwa ndi munthu iwe, Unenere za aneneri a Israyeli onenerawo, nuziti nao onenera za m'mtima mwao mwao, Tamverani mau a Yehova.

3. Atero Ambuye Yehova, Tsoka aneneri opusawo akutsata mzimu wao wao, cinkana sanaona kanthu.

4. Aneneri ako, Israyeli, akhala ngati nkhandwe m'mapululu.

Ezekieli 13