17. Mfumu nibweza mau kwa Rehumu ciwinda ca malamulo, ndi kwa Simsai mlembi, ndi kwa anzao otsala okhala m'Samariya, ndi otsala tsidya lino la mtsinjewo, Mtendere, ndi nthawi yakuti.
18. Kalatayo mwatitumizira anandiwerengera momveka.
19. Ndipo ndinalamulira anthu, nafunafuna, napeza kuti mudzi uwu unaukira mafumu kuyambira kale lomwe ndi kuti akacitamo mpanduko ndi kudziyendera.
20. Panalinso mafumu amphamvu m'Yerusalemu amene anacita ufumu tsidya lija lonse la mtsinje, ndipo anthu anawapatsa msonkho, thangata, ndi msonkho wa m'njira.
21. Mulamulire tsono kuti anthu awa aleke, ndi kuti asamange mudzi uwu, mpaka ndidzalamulira ndine.
22. Cenjerani mungadodomepo, cidzakuliranji cisauko ca kusowetsa mafumu?