Ezara 2:61-64 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

61. Ndi ana a ansembe: ana a Habaya, ana a Kozi, ana a Barizilai, amene anadzitengera mkazi wa ana akazi a Barizilai Mgileadi, nachedwa dzina lao.

62. Awa anafunafuna maina ao m'buku la iwo owerengedwa mwa cibadwidwe cao, koma osawapeza; potero anacotsedwa ku nchito ya nsembe monga odetsedwa.

63. Ndipo kazembe anawauza kuti asadyeko zopatulikitsa, mpaka adzabuka wansembe wokhala ndi Urimu ndi Tumimu.

64. Msonkhano wonse pamodzi ndiwo wa zikwi makumi anai ndi awiri mphambu mazana atatu kudza makumi asanu ndi limodzi,

Ezara 2