Ezara 1:6-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo onse akuwazinga analimbitsa manja ao ndi zipangizo za siliva, ndi golidi, ndi cuma, ndi zoweta, ndi zinthu za mtengo wace, pamodzi ndi nsembe zaufulu.

7. Koresi mfumu anaturutsanso zipangizo za nyumba ya Yehova, zimene Nebukadinezara adaziturutsa m'Yerusalemu, ndi kuziika m'nyumba ya milungu yace;

8. zomwezi Koresi mfumu ya ku Perisiya anaziturutsa ndi dzanja la Miteridati wosunga cumayo, naziwerengera Sezibazara kalonga wa Ayuda.

9. Kuwerenga kwace ndiko: mbizi zagolidi makumi atatu, mbizi zasiliva cikwi cimodzi, mipeni makumi awiri mphambu isanu ndi inai;

Ezara 1