Estere 3:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Zitatha izi, mfumu Ahaswero anamkuza Hamani mwana wa Hamedata, wa ku Agagi, namkweza, naika mpando wace upose akalonga onse okhala naye.

2. Ndipo anyamata onse a mfumu okhala m'cipata ca mfumu anamweramira, namgwadira Hamani; pakuti mfumu idalamulira cotero za iye. Koma Moredekai sanamweramira kapena kumgwadira.

3. Ndipo anyamata a mfumu okhala m'cipata ca mfumu anati kwa Moredekai, Ulakwiranji pa lamulo la mfumu?

Estere 3