Eksodo 9:23-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Pamenepo Mose anasamulira ndodo yace kuthambo, ndipo Yehova anatumiza bingu ndi matalala, ndi moto unatsikira pansi; ndipo Yehova anabvumbitsa matalala pa dziko la Aigupto.

24. Potero panali matalala, ndi mota wakutsikatsika pakati pa matalala, coopsa ndithu; panalibe cotere m'dziko lonse la Aigupto ciyambire mtundu wao.

25. Ndipo matalala anapanda m'dziko lonse la Aigupto zonse za pabwalo, kuyambira anthu kufikira zoweta; ndipo matalala anapanda zitsamba zonse za kuthengo, nathyola mitengo yonse ya kuthengo.

26. M'dziko la Goseni mokha, mokhala ana a Israyeli, munalibe matalala.

Eksodo 9