Eksodo 40:21-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. nalowa nalo likasa m'kacisi, napacika nsaru yocinga, nacinga likasa la mboni; monga Yehova adamuuza Mose.

22. Ndipo anaika gomelo m'cihema cokomanako, pa mbali ya kumpoto ya kacisi, kunja kwa nsaru yocinga.

23. Nakonzerapo mkate pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

24. Ndipo anaika coikapo nyali m'cihema cokomanako, popenyana ndi gome, pa mbali ya kumwela ya kacisi.

25. Nayatsa nyalizo pamaso pa Yehova; monga Yehova adamuuza Mose.

26. Ndipo anaika guwa la nsembe lagolidi m'cihema cokomanako cakuno ca nsaru yocinga;

27. nafukizapo cofukiza ca pfungo lokoma; monga Yehova adamuuza Mose.

28. Ndipo anapacika kukacisi nsaru yotsekera pakhomo.

Eksodo 40