24. ndi kida mazana asanu, monga sekeli la malo opatulika, ndi mafuta a azitona hini limodzi;
25. ndipo ukonze nazo mafuta odzoza opatulika, osanganizika monga mwa macitidwe a wosanganiza; akhale mafuta odzoza opatulika.
26. Ndipo udzoze nao cihema cokomanako, ndi likasa la mboni,
27. ndi gomelo ndi zipangizo zace zonse, ndi coikapo nyali ndi zipangizo zace,
28. ndi guwa la nsembe lofukizapo, ndi guwa la nsembe yopsereza ndi zipangizo zace zonse, ndi mkhate wosambiramo ndi tsinde lace.
29. Ndipo uzipatule, kuti zikhale zopatulika ndithu; zonse zakuzikhudza zidzakhala zopatulika.
30. Ndipo udzoze Aroni ndi ana ace amuna, ndi kuwapatula andicitire nchito ya nsembe.