Eksodo 16:27-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Ndipo kunali tsiku la Sabata, kuti anthu ena anaturuka kukaola, koma sanaupeza.

28. Ndipo Yehova anati kwa Mose, Mukana kusunga zouza zanga ndi malamulo anga kufikira titi?

29. Taonani, popeza Yehova anakupatsani Sabata, cifukwa cace tsiku lacisanu ndi cimodzi alikupatsa inu mkate wofikira masiku awiri; khalani yense m'malo mwace, munthu asaturuke m'malo mwace tsiku lacisanu ndi ciwiri.

30. Ndipo anthu anapumula tsiku lacisanu ndi ciwiri.

31. Ndipo mbumba ya Israyeli inaucha dzina lace Mana; ndiwo ngati zipatso zampasa, oyera; powalawa akunga timitanda tosanganiza ndi uci.

Eksodo 16