Eksodo 12:43-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

43. Ndipo Yehova anati kwa Mose ndi Aroni, Lemba la Paskha ndi ili: mwana wa mlendo ali yense asadyeko;

44. koma kapolo wa mwini ali yense, wogula ndi ndarama, utamdula, ndipo adyeko.

45. Mlendo kapena wolembedwa nchito asadyeko.

46. Audye m'nyumba imodzi; usaturukira nayo kubwalo nyama yina; ndipo musathyole pfupa lace.

47. Msonkhano wonse wa Israyeli uzicita ici.

48. Koma akakhala nanu mlendo, nakonzera Yehova Paskha, adulidwe amuna ace onse, ndipo pamenepo asendere kuucita; nakhale ngati wobadwa m'dziko; koma wosadulidwa ali yense asadyeko.

Eksodo 12