43. Ndipo Yehova anati kwa Mose ndi Aroni, Lemba la Paskha ndi ili: mwana wa mlendo ali yense asadyeko;
44. koma kapolo wa mwini ali yense, wogula ndi ndarama, utamdula, ndipo adyeko.
45. Mlendo kapena wolembedwa nchito asadyeko.
46. Audye m'nyumba imodzi; usaturukira nayo kubwalo nyama yina; ndipo musathyole pfupa lace.
47. Msonkhano wonse wa Israyeli uzicita ici.
48. Koma akakhala nanu mlendo, nakonzera Yehova Paskha, adulidwe amuna ace onse, ndipo pamenepo asendere kuucita; nakhale ngati wobadwa m'dziko; koma wosadulidwa ali yense asadyeko.