26. Ndipo kudzakhala, pamene ana anu adzanena ndi inu, Kutumikiraku muli nako nkutani?
27. mudzati, Ndiko nsembe ya Paskha wa Yehova, amene anapitirira nyumba za ana a Israyeli m'Aigupto, pamene anakantha Aaigupto, napulumutsa nyumba zathu.
28. Ndipo anthu anawerama, nalambira. Ndipo ana a Israyeli anamuka nacita monga Yehova adalamulira Mose ndi Aroni; anacita momwemo.
29. Ndipo panakhala pakati pa usiku, Yehova anakantha ana oyamba onse a m'dziko la Aigupto, kuyambira mwana woyamba wa Earao wakukhala pa mpando wacifumu wace kufikira mwana woyamba wa wam'nsinga ali m'kaidi; adi ana oyamba onse a zoweta.