Deuteronomo 32:44-48 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Ndipo anadza Mose nanena mau onse a nyimbo iyi m'makutu mwa anthu, iye, ndi Hoseya mwana wa Nuni.

45. Ndipo Mose anatha kunena mau awa onse kwa Israyeli wonse;

46. nati nao, Ikani mitima yanu pa mau onse ndikucitirani nao mboni lero; kuti muuze ana anu asamalire kuwacita mau onse a cilamulo ici.

47. Pakuti sicikhala kwa inu cinthu copanda pace, popeza ndico moyo wanu, ndipo mwa cinthu ici mudzacurukitsa masiku anu m'dziko limene muolokera Yordano, kulilandira.

48. Ndipo Yehova ananena ndi Mose tsiku lomweli, ndi kuti,

Deuteronomo 32