Deuteronomo 30:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ndipo silikhala tsidya la nyanja, kuti mukati, Adzatiolokera ndani tsidya la nyanja, ndi kutitengera ili, ndi kutimvetsa ili, kuti tilicite?

14. Pakuti mauwa ali pafupifupi ndi inu, m'kamwa mwanu, ndi m'mtima mwanu, kuwacita.

15. Tapenyani, ndaika pamaso panu lero lino moyo ndi zokoma, imfa ndi zoipa;

16. popeza ndikuuzani lero kukonda Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace, ndi kusunga malamulo ace ndi malemba ace ndi maweruzo ace, kuti mukakhale ndi moyo ndi kucuruka, ndi kuti Yehova Mulungu wanu akakudalitseni m'dziko limene mulowako kulilandira.

Deuteronomo 30