Deuteronomo 29:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pakuti mudziwa cikhalidwe cathu m'dziko la Aigupto, ndi kuti tinapyola pakati pa amitundu amene munawapyola;

17. ndipo munapenya zonyansa zao, ndi mafano ao, mtengo ndi mwala, siliva ndi golidi, zokhala pakati pao;

18. kuti angakhale pakati pa inu mwamuna, kapena mkazi, kapena banja, kapena pfuko, mtima wao watembenuka kusiyana naye Yehova Mulungu wathu lero lino, kuti apite ndi kutumikira milungu ya amitundu aja; kuti ungakhale pakati pa inu muzu wakubala ndulu ndi cowawa.

19. Ndipo kungakhale, akamva mau a lumbiro ili adzadzidalitsa m'mtima mwace, ndi kuti, Ndidzakhala nao mtendere, ndingakhale ndiyenda nao mtima wanga wopulukira, kuledzera nditamva ludzu;

20. Yehova sadzamkhululukira, koma pamenepo mkwiyo wa Yehova ndi nsanje yace zidzamfukira munthuyo; ndipo temberero lonse lolembedwa m'buku ili lidzamkhalira; ndipo Yehova adzafafaniza dzina lace pansi pa thambo.

Deuteronomo 29