2. ndipo madalitso awa onse adzakugwerani, ndi kukupezani, mukadzamvera mau a Yehova Mulungu wanu.
3. Mudzakhala odala m'mudzi, ndi odala kubwalo.
4. Zidzakhala zodala zipatso za thupi lanu, ndi zipatso za nthaka yanu, ndi zipatso za zoweta zanu, zoswana za ng'ombe zanu, ndi zoswana za nkhosa zanu.
5. Zidzakhala zodala mtanga wanu, ndi coumbiramo mkate wanu.