2. Ndipo muziphera Yehova Mulungu wanu nsembe ya Paskha, ya nkhosa ndi ya ng'ombe, m'malo amene Yehova adzasankha kukhalitsamo dzina lace.
3. Musamadyera nayo mkaye wa cotupitsa; masiku asanu ndi awiri mudyere nayo mkate wopanda cotupitsa, ndiwo mkate wa cizunziko popeza munaturuka m'dziko la Aigupto mofulumira; kuti inu kumbukile tsiku loturuka inu m'dziko la Aigupto masiku onse a moyo wanu.
4. Ndipo m'malire mwanu monse musaoneke cotupitsa masiku asanu ndi awiri; nyama yomwe muiphere nsembe tsiku loyamba madzulo, isatsaleko usiku wonse kufikira m'mawa.
5. Simuyenera kuphera nsembe ya Paskha m'midzi yanu iri yonse, imene Yehova Mulungu wanu akupatsani;