Deuteronomo 11:18-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Cifukwa cace muzisunga mau anga awa mumtima mwanu ndi m'moyo mwanu; ndi kuwamanga ngati cizindikilo pamanja panu; ndipo zikhale zapamphumi pakati pa maso anu.

19. Ndipo muziwaphunzitsa ana anu, ndi kuwalankhula awa pokhala inu pansi m'nyumba mwanu, ndi poyenda inu panjira, ndi pogona inu pansi, ndi pakuuka inu pomwe.

20. Ndipo muziwalembera pa mphuthu za nyumba zanu, ndi pa zipata zanu;

21. kuti masiku anu ndi masiku a ana anu acuruke m'dziko limene Yehova analumbira kwa makolo anu kuti adzawapatsali, monga masiku a thambo liri pamwamba pa dziko.

Deuteronomo 11