Deuteronomo 10:11-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo Yehova anati kwa ine, Uka, tenga ulendo pamaso pa anthu; kuti alowe ndi kulandira dzikoli ndinalumbirira makolo ao kuti ndidzawapatsa.

12. Ndipo tsopano, Israyeli, Yehova Mulungu wanu afunanji nanu, koma kuti muziopa Yehova Mulungu wanu, kuyenda m'njira zace zonse, ndi kukonda, ndi kutumikira Yehova Mulungu wanundimtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse,

13. kusunga malamulo a Yehova, ndi malemba ace, amene ndikuuzani lero kuti kukukomereni inu?

Deuteronomo 10