Danieli 9:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Caka coyamba ca Dariyo mwana wa Ahaswero, wa mbeu ya Amedi, amene anamlonga mfumu ya Akasidi;

2. caka coyamba ca ufumu wace, ine Danieli ndinazindikira mwa mabuku kuti ciwerengo cace ca zaka, cimene mau a Yehova anadzera naco kwa Yeremiya mneneri, kunena za makwaniridwe a mapasuko a Yerusalemu, ndizo zaka makumi asanu ndi awiri.

3. Ndipo ndinaika nkhope yanga kwa Ambuye Mulungu, kumfunsa Iye m'pemphero, ndi mapembedzero, ndi kusala, ndi ziguduli, ndi mapulusa.

Danieli 9