26. Koma woweruza mlandu adzakhalako, ndipo adzacotsa ulamuliro wace, kuutha ndi kuuononga kufikira cimariziro.
27. Ndipo ufumu, ndi ulamuliro, ndi ukulu wa maufumu, pansi pa thambo lonse, zidzapatsidwa kwa anthu a opatulika a Wam'mwambamwamba; ufumu wace ndiwo ufumu wosatha, ndi maiko onse adzamtumikira ndi kummvera.
28. Kutha kwace kwa cinthuci nkuno. Ine Danieli, maganizo anga anandibvuta kwambiri, ndi nkhope yanga inasandulika; koma ndinasunga cinthuci m'mtima mwanga.