Danieli 7:26-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Koma woweruza mlandu adzakhalako, ndipo adzacotsa ulamuliro wace, kuutha ndi kuuononga kufikira cimariziro.

27. Ndipo ufumu, ndi ulamuliro, ndi ukulu wa maufumu, pansi pa thambo lonse, zidzapatsidwa kwa anthu a opatulika a Wam'mwambamwamba; ufumu wace ndiwo ufumu wosatha, ndi maiko onse adzamtumikira ndi kummvera.

28. Kutha kwace kwa cinthuci nkuno. Ine Danieli, maganizo anga anandibvuta kwambiri, ndi nkhope yanga inasandulika; koma ndinasunga cinthuci m'mtima mwanga.

Danieli 7