Danieli 6:18-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Pamenepo mfumu inamuka ku cinyumba cace, nicezera kusala usikuwo, ngakhale zoyimbitsa sanabwera nazo pamaso pace, ndi m'maso mwace munamuumira.

19. Nilawira mamawa mfumu, nimuka mofulumira ku dzenje la mikango.

20. Ndipo poyandikira padzenje inapfuula ndi mau acisoni mfumu, ninena, niti kwa Danieli, Danieli, mnyamata wa Mulungu wamoyo, kodi Mulungu wako, amene umtumikira kosalekeza, wakhoza kukulanditsa kwamikango?

21. Pamenepo Danieli anati kwa mfumu, Mfumu, mukhale ndi moyo cikhalire.

22. Mulungu wanga watuma mthenga wace, natseka pakamwa pa mikango; ndipo siinandipweteka, cifukwa anandiona wosacimwa pamaso pace, pamaso panunso, mfumu, sindinalakwa.

Danieli 6