Danieli 5:13-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Pamenepo analowa naye Danieli kwa mfumu. Mfumu inayankha, niti kwa Danieli, Ndiwe kodi Danieli uja wa ana a ndende a Yuda, amene mfumu atate wanga anatenga ku Yuda?

14. Ndamva za iwe kuti muli mzimu wa milungu mwa iwe, ndi kuti mupezeka mwa iwe kuunika, ndi luntha, ndi nzeru zopambana.

15. Ndipo tsono anabwera nao kwa ine anzeru, openda, kuti awerenge lemba ilo, ndi kundidziwitsa kumasulira kwace; koma sanakhoza kufotokozera kumasulira kwa cinthuci.

Danieli 5